86. Malamulo anu onse ngokhulupirika;Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.
87. Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.
88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,
89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.
90. Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.