65. Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova,Monga mwa mau anu.
66. Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru;Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.
67. Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.
68. Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino;Mundiphunzitse malemba anu.
69. Odzikuza anandipangira bodza:Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70. Mtima wao unona ngati mafuta;Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.