6. Pamenepo sindidzacita manyazi,Pakupenyerera malamulo anu onse.
7. Ndidzakuyanrikani ndi mtima woongoka,Pakuphunzira maweruzo anu olungama.
8. Ndidzasamalira malemba anu:Musandisiye ndithu.
9. Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ace bwanji?Akawasamalira monga mwa mau anu.
10. Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse;Ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.
11. Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga,Kuti ndisalakwire Inu.
12. Inu ndinu wodala Yehova;Ndiphunzitseni malemba anu.
13. Ndinafotokozera ndi milomo yangaMaweruzo onse a pakamwa panu,
14. Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,
15. Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.
16. Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu;Sindidzaiwala mau anu,
17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.