38. Limbitsirani mtumiki wanu mau anu,Ndiye wodzipereka kukuopani.
39. Mundipatutsire cotonza canga ndiciopaco;Popeza maweruzo anu ndi okoma.
40. Taonani, ndinalira malangizo anu;Mundipatse moyo mwa cilungamo canu.
41. Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova,Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.