27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.
28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.
29. Mundicotsere njira ya cinyengo;Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.
30. Ndinasankha njira yokhulupirika;Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,
31. Ndimamatika nazo mboni zanu;Musandicititse manyazi, Yehova.