18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.
19. Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;Musandibisire malamulo anu.
20. Mtima wanga wasweka ndi kukhumbaMaweruzo anu nyengo zonse.
21. Munadzudzula odzikuza otembereredwa,Iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.
22. Mundicotsere cotonza, ndi cimpepulo;Pakuti ndinasunga mboni zanu.
23. Nduna zomwe zinakhala zondineneza;Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.
24. Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.