17. Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo;Ndipo ndidzasamalira mau anu.
18. Munditsegulire maso, kuti ndipenyeZodabwiza za m'cilamulo canu.
19. Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;Musandibisire malamulo anu.
20. Mtima wanga wasweka ndi kukhumbaMaweruzo anu nyengo zonse.
21. Munadzudzula odzikuza otembereredwa,Iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.
22. Mundicotsere cotonza, ndi cimpepulo;Pakuti ndinasunga mboni zanu.
23. Nduna zomwe zinakhala zondineneza;Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.
24. Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa,Ndizo zondipangira nzeru.
25. Moyo wanga umamatika ndi pfumbi;Mundipatse moyo monga mwa mau anu.
26. Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha:Mundiphunzitse malemba anu.
27. Mundizindikiritse njira ya malangizo anu;Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.
28. Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni:Mundilimbitse monga mwa mau anu.