136. Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi,Popeza sasamalira cilamulo canu.
137. Inu ndinu wolungama, Yehova,Ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.
138. Mboni zanuzo mudazilamuliraZiri zolungama ndi zokhulupirika ndithu.
139. Cangu canga cinandithera,Popeza akundisautsa anaiwala mau anu.
140. Mau anu ngoyera ndithu;Ndi mtumiki wanu awakonda.
141. Wamng'ono ine, ndi wopepulidwa;Koma sindiiwala malemba anu.