126. Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu;Pakuti anaswa cilamulo canu.
127. Cifukwa cace ndikonda malamulo anuKoposa golidi, Inde golidi woyengeka,
128. Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse;Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.
129. Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,
130. Potsegulira mau anu paunikira;Kuzindikiritsa opusa.
131. Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu;Popeza ndinakhumba malamulo anu.
132. Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo,Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.
133. Kfiazikitsanimapaziangam'mau anu;Ndipo zisandigonjetse zopanda pace ziri zonse.
134. Mundiombole ku nsautso ya munthu:Ndipo ndidzasamalira malangizo anu.
135. Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu;Ndipo mundiphunzitse malemba anu.