11. Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga,Kuti ndisalakwire Inu.
12. Inu ndinu wodala Yehova;Ndiphunzitseni malemba anu.
13. Ndinafotokozera ndi milomo yangaMaweruzo onse a pakamwa panu,
14. Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu,Koposa ndi cuma conse,
15. Ndidzalingirira pa malangizo anu,Ndi kupenyerera mayendedwe anu.