102. Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.
103. Mau anu azunadi powalawa ine!Koposa uci m'kamwa mwanga.
104. Malangizo anu andizindikiritsa;Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,
105. Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga,Ndi kuunika kwa panjira panga,
106. Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima,Kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.