14. Yehova akuonjezereni dalitso, Inu ndi ana anu.
15. Odalitsika inu a kwa Yehova,Wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16. Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova;Koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.
17. Akufa salemekeza Yehova,Kapena ali yense wakutsikira kuli cete:
18. Koma ife tidzalemekeza YehovaKuyambira tsopano kufikira nthawi yonse.Haleluya.