23. Iwo akutsikira kunyanja nalowa m'zombo,Akucita nchito zao pa madzi akuru;
24. Iwowa apenya nchito za Yehova,Ndi zodabwiza zace m'madzi ozama.
25. Popeza anena, nautsa namondwe,Amene autsa mafunde ace.
26. Akwera kuthambo, atsikira kozama;Mtima wao usungunuka naco coipaco.
27. Adzandira napambanitsa miyendo ngati munthu woledzeta,Nathedwa nzeru konse.