8. Akumbukila cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;
9. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;
10. Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.
11. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
12. Pokhala iwo anthu owerengeka,Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
13. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
14. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;
15. Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga.
16. Ndipo anaitana njala igwere dziko;Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.
17. Anawatsogozeratu munthu;Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:
18. Anapweteka miyendo yace ndi matangadza;Anamgoneka m'unyolo;
19. Kufikira nyengo yakucitika maneno ace;Mau a Yehova anamuyesa.
20. Mfumuyo anatuma munthu nammasula;Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.
21. Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace,Ndi woweruza wa pa zace zonse: