3. Mudzitamandire ndi dzina lace loyera:Mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.
4. Funani Yehova, ndi mphamvu yace;Funsirani nkhope yace nthawi zonse.
5. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita;Zizindikilo zace ndi maweruzo a pakamwa pace;
6. Inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.
7. Iye ndiye Yehova, Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi.
8. Akumbukila cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;
9. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;