9. Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,
10. Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu;Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.
11. Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;Ndipo ine ndauma ngati udzu.
12. Koma Inu, Yehova, mukhalabe ku nthawi yonse;Ndi cikumbukilo canu ku mibadwo mibadwo.
13. Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni;Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.