21. Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni,Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;
22. Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,Ndi maufumu kuti atumikire Yehova.
23. Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.
24. Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga:Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.
25. Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.