1. Yehova, imvani pemphero langa,Ndipo mpfuu wanga ufikire Inu.
2. Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga;Mundichereze khutu lanu;Tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga,
3. Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi,Ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.
4. Mtima wanga ukunga udzu wamweta, nufota;Popeza ndiiwala kudya mkate wanga.
5. Cifukwa ca liu la kubuula kwangaMnofu wanga umamatika ku mafupa anga.
6. Ndikunga bvuwo m'cipululu;Ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.