9. Alalira monga mkango m'ngaka mwace;Alalira kugwira wozunzika:Agwira wozunzika, pakumkola m'ukonde mwace.
10. Aunthama, nawerama,Ndipo aumphawi agwa m'zala zace.
11. Anena m'mtima mwace, Mulungu waiwala;Wabisa nkhope yace; sapenya nthawi zonse,
12. Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu;Musaiwale ozunzika.
13. Woipa anyozeranii Mulungu,Anena m'mtima mwace, Simudzafunsira?
14. Mwapenya; pakuti mumayang'anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m'manja mwanu;Waumphawi adzipereka kwa Inu;Wamasiye mumakhala mthandizi wace.
15. Thyolani mkono wa woipa;Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.
16. Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya;Aonongeka amitundu m'dziko lace.
17. Yehova, mwamva cikhumbo ca ozunzika:Mudzakhazikitsa mtima wao, mudzachereza khutu lanu:
18. Kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi,Kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.