4. Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira.Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.
5. Mayendedwe ace alimbika nthawi zonse;Maweruzo anu ali pamwamba posaona iye;Adani ace onse awanyodola.
6. Ati mumtima mwace, Sindidzagwedezeka ine;Ku mibadwo mibadwo osagwa m'tsoka ine.
7. M'kamwa mwace mwadzala kutemberera ndi manyengo ndi kucenjerera;Pansi pa lilime lace pali cibvutitso copanda pace.
8. Akhala m'molalira midzi;Mobisalamo akupha munthu wosacimwa:Ambisira waumphawi nkhope yace,
9. Alalira monga mkango m'ngaka mwace;Alalira kugwira wozunzika:Agwira wozunzika, pakumkola m'ukonde mwace.
10. Aunthama, nawerama,Ndipo aumphawi agwa m'zala zace.