26. Ndipo musamadya mwazi uti wonse, kapena wa mbalame, kapena wa nyama, m'nyumba zanu zonse,
27. Ali yense akadya mwazi uti wonse, munthuyo asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.
28. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
29. Lankhula ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Wakubwera nayo nsembe yoyamika yace kwa Yehova, azidza naco copereka cace kwa Yehova cocokera ku nsembe yoyamika yace;
30. adze nazo m'manja mwace nsembe zamoto za Yehova; adze nao mafuta pamodzi ndi nganga, kuti aweyule ngangayo ikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
31. Ndipo wansembeyo atenthe mafutawo pa guwa la nsembe; koma ngangayo ikhale ya Arent ndi ana ace.
32. Ndipo mwendo wathako wa ku dzanja lamanja muupereke kwa wansembe, ukhale nsembe yokweza yocokera ku nsembe zoyamika zanu.