52. Ndipo zikamtsalira zaka pang'ono kufikira caka coliza lipenga amwerengere; monga mwa zaka zace abwezere mtengo wace wakumuombola.
53. Akhale naye monga wolipidwa caka ndi caka; asamamlamulira momzunza pamaso pako,
54. Ndipo akapanda kumuombola motero, azituruka caka coliza lipenga, iye ndi ana ace omwe.
55. Pakuti ana a Israyeli ndi atumiki anga; iwo ndiwo atumiki anga amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.