3. Ali yense aopemai wace, ndi atate wace; nimusunge masabata anga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4. Musamatembenukira mafano, kapena kudzipangira mulungu woyenga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5. Ndipo pamene muphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandiridwe.
6. Tsiku lomwelo mwaipha, ndi m'mawa mwace muidye; ngati katsalirako kanthu tsiku lacitatu, muzikatentha ndi moto.
7. Akakadya konse tsiku tacitatu kali conyansa, kosabvomerezeka: