10. Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.
11. Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.
12. Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.
13. Usamabvula mbale wa mai wako; popeza ndiye mbale wa mai wako.
14. Usamabvula mbale wa atate wako; usamasendera kwa mkazi wace; ndiye mai wako.