35. Ndipo anamwetsa vinyo atate wao usiku womwenso; wamng'ono ndipo anauka nagona naye; ndipo iye sanadziwa pomwe anagona ndi pomwe anauka.
36. Ndipo ana akazi awiri a Loti anali ndi pakati pa atate wao.
37. Woyamba ndipo anabala mwana wamwamona, namcha dzina lace. Moabu; yemweyo ndi atate wa Amoabu kufikira lero.
38. Wamng'ono ndipo anabala mwana wamwamuna, namcha dzina lace Benammi; yemweyo ndi atate wa Aamoni kufikira lero.