23. Ndi ana a Aramu: Uzi ndi Huli, ndi Getere, ndi Masi.
24. Aripakasadi ndipo anabala Sela; ndipo Sela anabala Ebere.
25. Kwa Ebere ndipo kunabadwa ana amuna awiri; dzina la wina ndi Pelege; cifukwa kuti m'masiku ace dziko lapansi linagawanikana; dzina la mphwace ndi Yokitani.
26. Ndipo Yokitani anabala Alamodadi, ndi Selefe, ndi Hazaramaveti, ndi Yera;
27. ndi Hadorimu ndi Uzali, ndi Dikila;
28. ndi Obali, ndi Abimaele, ndi Sheva;
29. ndi Ofiri ndi Havila, ndi obabi; onse amenewa ndi ana a okitani.
30. Kwao kunayamba pa Mesa pakunka ku Sefere phiri la kum'mawa.
31. Amenewa ndi ana a Semu, monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.
32. Amenewo ndi mabanja a ana a Nowa monga mwa mibadwo yao, m'mitundu yao: ndi amenewo anagawanika mitundu pa dziko lapansi, citapita cigumula.