1. PACIYAMBI Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2. Dziko lapansi ndipo linali lopanda kanthu; ndipo mdima unali pamwamba pa nyanja; ndipo mzimu wa Mulungu unaliokufungatira pamwamba pa madzi.
3. Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.
4. Ndipo anaona Mulungu kuti kuyerako kunali kwabino: ndipo Mulungu analekanitsa kuyera ndi mdima.