6. golidi, ndi siliva, ndi mkuwa; ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;
7. ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;
8. ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;
9. ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.
10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;
11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;
12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;
13. gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;
14. ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;