1. Za amisiri opanga nchitoyi, Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2. Taona ndaitana ndi kumchula dzina lace, Bezaleli, mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa pfuke la Yuda;
3. ndipo ndamdzaza nd mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, ndi m'nchito ziri zonse,
4. kulingirira nchito zaluso, kucita ndi golidi ndi siliva ndi mkuwa,