1. Usatola mbiri yopanda pace; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yocititsa ciwawa.
2. Usatsata unyinji wa anthu kucita coipa; kapena usacita umboni kumlandu, ndi kupatukira kutsata unyinji ndi kukhotetsa mlandu;
3. kapena usakometsera munthu wosauka pa mlandu wace.