1. Munthu akaba ng'ombe, kapena nkhosa, nakaipha, kapena kuigulitsa, azilipa ng'ombe zisanu pa ng'ombeyo; ndi nkhosa zinai pa nkhosayo,
2. Akampeza wakuba alimkuboola, nakamkantha kotero kuti wafa, palibe camwazi.
3. Litamturukira dzuwa, pali camwazi; wakubayo azilipa ndithu; ngati alibe kanthu, amgulitse pa umbala wace.