9. Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ace; ndi ana a Israyeli anamvera iye, nacita monga Yehova adauza Mose.
10. Ndipo sanaukanso mnereri m'lsrayeli ngati Mose, amene Yehova anadziwana naye popenyana maso;
11. kunena za zizindikilo ndi zozizwa zonse zimene Yehova anamtumiza kuzicita m'dziko la Aigupto kwa Farao, ndi anyamata ace onse, ndi dziko lace lonse;
12. ndi kunena za dzanja la mphamvu lonse, ndi coopsa cacikuru conse, cimene Mose anacita pamaso pa Israyeli wonse.