13. Ndipo za Yosefe anati,Yehova adalitse dziko lace;Ndi zinthu zofunikatu za m'mwamba, ndi mame,Ndi madzi okhala pansipo;
14. Ndi zipatso zofunikatu za dzuwa,Ndi zomera zofunikatu za mwezi,
15. Ndi zinthu zoposa za mapiri akale,Ndi zinthu zofunikatu za zitunda zosatha,