10. koma ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba musamadya; muziyese zonyansa.
11. Mbalame zosadetsazonse muyenera kumadya.
12. Koma izi ndi zimene simuyenera kumadya: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi,
13. ndi kamtema, ndi mphamba, ndi muimba monga mwa mtundu wace;
14. ndi khungubwe ali yense monga mwa mtundu wace;
15. ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi monga mwa mtundu wace;
16. ndi nkhutukutu, ndi mancici, ndi tsekwe;
17. ndi bvuwo, ndi dembu, ndi nswankhono;
18. ndi iodwa, ndi cimeza, monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.