23. Iye ndiye waulemu koposa makumi atatuwo, koma sadafikana ndi atatu oyamba. Ndipo Davide anamuika kuyang'anira olindirira ace.
24. Asaheli mbale wa Yoabu anali wa makumi atatuwo; Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu;
25. Sama Mharodi, Elika Mharodi;
26. Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi Mtekoi.
27. Abiyezeri M-anetori, Mebunai Mhusati;
28. Zalimoni M-ahohi, Maharai Mnefati;
29. Helebi mwana wa Baana Mnetofati, ltai mwana wa Ribai wa ku Gibeya wa ana a Benjamini;
30. Benaya Mpiratoni, Hidai wa ku timitsinje ta Gaasi;
31. Abialiboni M-aribati, Azmaveti Mbahurimi;
32. Eliaba Mshaliboni wa ana a Jaseni, Jonatani;
33. Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari;
34. Elifaleti mwana wa Ahasibai, mwana wa Mmaacha, Eliamu mwana wa Ahitofeli Mgiloni;
35. Hezra wa ku Karimeli, Paarai M-aribi;
36. Igali mwana wa Natani wa ku Zoba, Bani Mgadi;
37. Zeleki M-amoni, Naharai Mbeeroti, onyamula zida za Yoabu mwana wa Zeruya;
38. Ira M-itri, Garebi M-itri;
39. Uriya Mhiti; onse pamodzi anali makumi atatu mphambu asanu ndi awiri.