1. Ndipo mau otsiriza a Davide ndi awa:—Atero Davide mwana wa Jese,Atero munthu wokwezedwa,Ndiye wodzozedwa wa Mulungu wa Yakobo,Ndi mwini masalmo wokoma wa Israyeli:
2. Mzimu wa Yehova unalankhula mwa ine,Ndi mau ace anali pa lilime langa,
3. Mulungu wa Israyeli anati,Thanthwe la Israyeli Gnalankhula ndi ine;Kudzakhala woweruza anthu molungama;Woweruza m'kuopa Mulungu.