1. Ndipo anauza Yoabu, Onani mfumu irikulira misozi, nilira Abisalomu.
2. Ndipo cipulumutso ca tsiku lila cinasandulika maliro kwa anthu onse; pakuti anthu anamva kuti, Mfumu iri ndi cisoni cifukwa ca mwana wace.
3. Ndipo tsiku lija anthu analowa m'mudzi kacetecete, monga azemba anthu akucita manyazi pakuthawa nkhondo.