25. Ndipo Peka mwana wa Remaliya, kazembe wace, anamcitira ciwembu, nawakantha limodzi mfumu ndi Arigobo ndi Ariye m'Samariya, m'nsanja ya ku nyumba ya mfumu; pamodzi ndi iye panali amuna makumi asanu a Gileadi; ndipo anamupha, nakhala mfumu m'malo mwace.
26. Macitidwe ena tsono a Pekahiya ndi zonse anazicita, taonani zalembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli.
27. Caka ca makumi asanu mphambu ziwiri ca Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya analowa ufumu wace wa Israyeli m'Samariya, nakhala mfumu zaka makumi awiri.