1. Ndipo Hana anapemphera, natiMtima wanga umyuka mokondwera kwa Yehova,Nyanga yanga yakwezeka mwa Yehova;Pakamwa panga pakula kwa adani anga;Popeza ndikondwera m'cipulumutsocanu.
2. Palibe wina woyera ngati Yehova;Palibe wina koma Inu nokha;Palibenso thanthwe longa Mulungu wathu.
3. Musalankhulenso modzikuza kwambiri motero;M'kamwa mwanu musaturuke zolulutsa;Cifukwa Yehova ali Mulungu wanzeru,Ndipo iye ayesa zocita anthu.