Natenga ng'ombe ziwiri nazidula nthuli nthuli, nazitumiza m'malire monse mwa Israyeli, ndi dzanja la mithenga, nati, Amene sakudza pambuyo pa Sauli ndi pa Samueli, adzatero nazo ng'ombe zace. Ndipo kuopsa kwa Yehova kunawagwera anthu, naturuka ngati munthu mmodzi.