23. Pakuti anadzimangiranso misanje, ndi zoimiritsa, ndi zifanizo, pa citunda conse cacitali, ndi patsinde pa mtengo wogudira uli wonse;
24. panalinso anyamata ocitirana dama m'dzikomo; iwo amacita monga mwa zonyansitsa za amitundu, amene Yehova anapitikitsa pamaso pa ana a Israyeli.
25. Ndipo kunacitika, Rebabiamu atakhala mfumu zaka zisanu, Sisaki mfumu ya Aigupto anakwera ndi nkhondo ku Yerusalemu,
26. nacotsa cuma ca m'nyumba ya Yehova, ndi cuma ca m'nyumba ya mfumu; inde anacotsa conseco, nacotsanso zikopa zagolidi zonse adazipanga Solomo.